ZOYENERA MU UZIMU (#13495)

Nenani: O Mulungu, Mulungu wanga! Bvekani mutu wanga ndi chisoti cha chilungamo, ndipo kongoletsani nkhope yanga ndi mchitidwe woongoka. Inu indetu, Ndinu Mwini mphatso ndi zaulere zonse.

-Bahá'u'lláh
-----------------------

ZOYENERA MU UZIMU (#13496)

O Mulungu! Tsitsimutsani ndi kusangalatsa mzimu wanga. Yeretsani mtima wanga. Walitsani mphamvu zanga. Ndikupereka zanga zonse m’dzanja Lanu. Inu ndiye Chitsogozo changa ndi Pothawira panga. Sindidzakhala wachisoni ndi wokhumudwa; Ndidzakhala munthu wokondwa ndi wosangalala. O Mulungu! Sindidzakhalanso ndi nkhawa, kapena kulola mabvuto kundigonjetsa. Sindidzakhala pa zinthu zosakondweretsa moyo.  
O Mulungu! Inu Ndinu bwenzi langa kwa ine kuposa m’mene ndiri ine kwa ine mwini. Ndikudzipereka kwa Inu, O Ambuye.

-`Abdu'l-Bahá
-----------------------

ZOYENERA MU UZIMU (#13497)

O Ambuye! Ndife wofooka; tilimbikitseni. O Mulungu! Ndife mbuli; tipangeni kukhala wozindikira. O Ambuye! Ndife amphawi; tipangeni kukhala wolemera. O Mulungu! Ndife akufa; titsitsimutseni. O Ambuye! Ndife wosayenerezeka konse; tipatseni ulemerero mu ufumu Wanu. Ngati mutithandiza, O Ambuye, tidzakhala ngati nyenyezi zothwanima. Ngati simutithandiza, tidzakhala wotsika kuposa dziko lapansi limene.  
O Ambuye! Tilimbikitseni. O Mulungu! Tipatseni kupambana. O Mulungu! Tithandizeni kugonjetsa kudzikonda ndi chilakolako. O Ambuye! Tipulumutseni ku nsinga za dziko lapansi. O Ambuye! Titsitsimutseni kupyolera mu kuuzira kwa Mzimu Woyera kuti tsono tithe kuchilimika ndi kukutumikirani, kukupembedzani, ndikudzipereka kwa thunthu mu ufumu Wanu ndi chikhulupiriro chonse.  
O Ambuye! Inu Ndinu Wamphamvu! O Mulungu, Inu 
Ndinu 	Wokhululukira! 	O 	Ambuye, 	Inu 	Ndinu 
Wosamalira!

-`Abdu'l-Bahá
-----------------------

